Yeremiya 46:4-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Mangani akavalo, bwerani, inu apakavalo, imani ndi zisoti zacitsulo; tuulani nthungo zanu, bvalani malaya acitsulo.

5. Cifukwa canji ndaciona? aopa, abwerera; amphamvu ao agwetsedwa, athawadi, osaceukira m'mbuyo; mantha ali ponseponse, ati Yehova.

6. Waliwiro asathawe, wamphamvu asapulumuke; kumpoto pambali pa nyanja ya Firate wapunthwa nagwa.

7. Ndani uyu amene auka ngati Nile, madzi ace ogabvira monga nyanja?

Yeremiya 46