Yeremiya 33:16-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Masiku omwewo Yuda adzapulumutsidwa, ndi Yerusalemu adzakhala mokhulupirika; ili ndi dzina adzachedwa nalo, Yehova ndiye cilungamo cathu.

17. Pakuti Yehova atero: Davide sadzasowa munthu wokhala pa mpando wacifumu wa nyumba ya Israyeli;

18. ndiponso ansembe sadzasowa munthu pamaso panga wakupereka nsembe zopsereza, ndi kutentha nsembe zaufa, ndi wakucita nsembe masiku onse.

19. Ndipo mau a Yehova anadza kwa Yeremiya, kuti,

20. Ngati mukhoza kuswa pangano langa la usana ndi pangano langa la usiku, kuti usakhalenso usana ndi usiku m'nyengo yao;

Yeremiya 33