Yeremiya 28:15-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Ndipo Yeremiya mneneri ananena kwa Hananiya mneneri, Tamvatu, Hananiya; Yehova sanakutuma iwe; koma ukhulupiritsa anthu awa zonama.

16. Cifukwa cace Yehova atero, Taona, Ine ndidzakucotsa iwe kudziko; caka cino udzafa, pakuti wanena zopikisana ndi Yehova.

17. Ndipo anafa Hananiya caka comweco mwezi wacisanu ndi ciwiri.

Yeremiya 28