Yeremiya 27:7-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Ndipo amitundu, onse adzamtumikira iye, ndi mwana wace, ndi mdzukulu wace, mpaka yafika nthawi ya dziko lace; ndipo amitundu ambiri ndi mafumu akuru adzamuyesa iye mtumiki wao.

8. Ndipo padzakhala, kuti mtundu ndi ufumu umene sudzamtumikira Nebukadinezara yemweyo mfumu ya ku Babulo, mtundu umenewo Ine ndidzalanga, ati Yehova, ndi lupanga, ndi njala, ndi caola, mpaka nditatha onse ndi dzanja lace.

9. Koma inu, musamvere aneneri anu, kapena akuombeza anu, kapena maloto anu, kapena alauli anu, kapena obwebweta anu, Musadzatumikira mfumu ya ku Babulo;

10. kakuti iwo akunenerani inu zonama, kuti akucotseni inu m'dziko lanu, kunka kutari kuti ndikupitikitseni inu, ndipo inu mudzathedwa.

Yeremiya 27