Yeremiya 23:1-2 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Tsoka abusa amene athetsa nabalalitsa nkhosa za busa langa! ati Yehova.

2. Cifukwa cace atero Yehova, Mulungu wa Israyeli, ponenera abusa amene adyetsa anthu anga: Mwabalalitsa zoweta zanga, ndi kuzipitikitsa, ndipo simunazizonda; taonani, ndidzakusenzani inu kuipa kwa nchito zanu, ati Yehova.

Yeremiya 23