Yeremiya 2:12-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Muzizwe pamenepo, miyamba inu, muope kwambiri, mukhale ouma, ati Yehova.

13. Pakuti anthu anga anacita zoipa ziwiri; anandisiya Ine kasupe wa madzi amoyo, nadziboolera zitsime, zitsime zong'aluka, zosakhalamo madzi.

14. Kodi Israyeli ndi mtumiki? kodi ndiye kapolo wobadwa m'nyumba? afunkhidwa bwanji?

15. Ana a mikango anambangulira iye, nakweza mau; anapasula dziko lace, midzi yace yatenthedwa, mulibenso wokhalamo.

Yeremiya 2