2. Cuma canu caola ndi zobvala zanu zajiwa ndi njenjete.
3. Golidi wanu ndi siliva wanu zacita dzimbiri, ndipo dzimbiri lace lidzacita mboni zoneneza Inu ndipo zidzadya nyama yanu ngat: moto. Mwadzikundikira cuma masiku otsiriza.
4. Taonani, mphotho ya anchitowo anasenga m'minda yanu, yosungidwa ndi inu powanyenga, ipfuula; ndipo mapfuulc a osengawo adalowa m'makutu a Ambuye wa makamu.
5. Mwadyerera padziko, ndipo mwacita zokukondweretsani; mwadyetsa mitima yanu m'tsiku lakupha.
6. Munamtsutsa, munapha wolungamayo, iye sakanizainu.