Tito 2:9-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Akapolo amvere ambuye ao a iwo okha, nawakondweretse m'zonse; osakana mau ao;

10. osatapa pa zao, komatu aonetsere cikhulupiriko conse cabwino; kuti akakometsere ciphunzitso ca Mpulumutsi wathu Mulungu m'zinthu zonse.

11. Pakuti caonekera cisomo ca Mulungu cakupulumutsa anthu onse,

12. ndi kutiphunzitsa ife kuti, pokana cisapembedzo ndi zilakolako za dziko lapansi, tikhale ndi moyo m'dziko lino odziletsa, ndi olungama, ndi opembedza;

Tito 2