5. Ndipo ananena naye, Zonse muzinena ndidzacita.
6. Pamenepo anatsikira popunthirapo, nacita zonse monga umo mpongozi wace adamuuza.
7. Ndipo atatha Boazi kudya ndi kumwa, nusekerera mtima wace, anakagona kuthungo kwa mulu wa tirigu; nadza iye kacetecete, nabvuodukula ku mapazi ace, nagona.
8. Ndipo kunali, pakati pa usiku munthuyo anadzidzimuka, natembenuka; ndipo taona pa mapazi ace pagona mkazi.