Rute 3:16-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Ndipo pamene anadza kwa mpongozi wace, iye anati, Wapeza bwanji, mwana wanga? Pamenepo anamfotokozera zonse anamcitira munthuyo.

17. Natinso, Miyeso iyi isanu ndi umodzi ya barele anandipatsa, pakuti anati, Usafike kwa mpongozi wako wopanda kanthu.

18. Ndipo anati, Khala ulipo, mwana wanga; mpaka udziwa umo ukhalire mlandu; pakuti munthuyo sadzauleka mpaka atautha mlanduwo lero lino.

Rute 3