9. Yehova akuloleni mupeze mpumulo yense m'nyumba ya mwamuna wace. Nawapsompsona, nakweza iwo mau ao nalira misozi.
10. Ndipo ananena naye, Iai, koma tidzapita nanu kwa anthu a kwanu.
11. Nati Naomi, Bwererani, ana anga, mudzatsagana nane bwanji? ngati ndiri nao m'mimba mwanga ana amuna ena kuti akhale amuna anu?