Rute 1:9-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Yehova akuloleni mupeze mpumulo yense m'nyumba ya mwamuna wace. Nawapsompsona, nakweza iwo mau ao nalira misozi.

10. Ndipo ananena naye, Iai, koma tidzapita nanu kwa anthu a kwanu.

11. Nati Naomi, Bwererani, ana anga, mudzatsagana nane bwanji? ngati ndiri nao m'mimba mwanga ana amuna ena kuti akhale amuna anu?

Rute 1