Oweruza 9:41-46 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

41. Ndipo Abimeleki anakhala ku Aruma; ndi Zebuli anafngitsa Gaala ndi abale ace kuti asakhale m'Sekemu.

42. Ndipo kunali m'mawa mwace, kuti anthu anaturuka kumka kuminda; ndipo anauza Abimeleki.

43. Pamenepo anatenga anthu, nawagawa magulu atatu, nalalira m'minda; napenya, ndipo taonani, anthu alimkuturuka m'mudzi; nawaukira iye nawakantha.

44. Ndi Abimeleki ndi magulu okhala naye anathamanga naima polowera pa cipata ca mudzi; ndi magulu awiriwo anagwera onse okhala m'munda, nawakantha.

45. Ndipo Abimeleki analimbana ndi mudzi tsiku lija lonse; nalanda mudzi nawapha anthu anali m'mwemo; napasula mudzi; nawazapo mcere.

46. Ndipo pamene eni ace onse a nsanja ya ku Sekemu anacimva, analowa m'ngaka ya nyumba ya Eliberiti.

Oweruza 9