21. Ndipo Ehudi anaturutsa dzanja lace lamanzere nagwira lupanga ku ncafu ya kulamanja nampyoza m'mimba mwace;
22. ndi cigumbu cace cinalowa kutsata mpeni wace; ndi mafuta anaphimba mpeniwo, pakuti sanasolola lupanga m'mimba mwace; nilituruka kumbuyo.
23. Pamenepo Ehudi anaturuka kukhonde namtsekera pamakomo pa cipinda cosanja nafungulira.
24. Ndipo ataturuka iye, anadza aka polo ace; napenya, ndipo taonani pamakomo pa cipinda cosanja mpofungulira; nati iwo, Angophimba mapazi m'cipinda cace cosanja copitidwa mphepo.
25. Ndipo analindirira mpaka anacita manyazi; koma taonani, sanatsegula pamakomo pa cipinda cosanja. Pamenepo anatenga mfungulo natsegula; ndipo taonani, mbuye wao wagwa pansi, wafa.
26. Ndipo Ehudi anapulumuka pakucedwa iwo, napitirira pa mafano osema, napulumuka kufikira Seira.
27. Ndipo kunali, pakufika iye anaomba lipenga ku mapiri a Efraimu; ndi ana a Israyeli anatsika naye kucokera kumapiri, nawatsogolera iye.
28. Ndipo ananena nao, Nditsateni ine, pakuti Yehova wapereka adani anu Amoabu m'manja mwanu. Ndipo anatsika ndi kumtsata, natsekereza Amoabu madooko a Yordano, osalola mmodzi aoloke.
29. Ndipo anakantha Amoabu nyengo ija anthu zikwi khumi, onsewa anthu amoyo, ndi ngwazi; ndipo sanapulumuka ndi mmodzi yense.
30. Motero anagonjetsa Moabu tsiku lija pansi pa dzanja la Israyeli. Ndipo dziko linapumulazaka makumi asanu ndi atatu.