Nyimbo 2:14-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Nkhunda yangawe, yokhala m'ming'alu ya thanthwe, mobisika motsetsereka,Ndipenye nkhope yako, ndimve manako;Pakuti mau ako ngokoma, nkhope yako ndi kukongola.

15. Mutigwirire ankhandwe, ngakhale ang'ono, amene akuononga minda yamipesa;Pakuti m'minda yathu yamipesa muphuka biriwiri.

16. Wokondedwa wanga ndi wa ine, ine ndine wace:Aweta zace pakati pa akakombo,

17. Mpaka dzuwa litapepa, mithunzi ndi kutanimpha,Bwera, bwenzi langawe, nukhale ngati mphoyo pena mwana wa mbawalaPa mapiri a mipata.

Nyimbo 2