Numeri 9:8-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Ndipo Mose ananena nao, Baimani; ndimve couza Yehova za inu.

9. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

10. Nena ndi ana a Israyeli, ndi kuti, Angakhale munthu wa inu kapena wa mibadwo yanu, adetsedwa, cifukwa ca mtembo, kapena pokhala paulendo, koma azicitira Yehova Paskha.

11. Mwezi waciwiri, tsiku lace lakhumi ndi cinai, madzulo, aucite; audye ndi mkate wopanda cotupitsa ndi msuzi wowawa.

Numeri 9