Numeri 8:6-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Uwatenge Alevi pakati pa ana a Israyeli, nuwayeretse.

7. Ndipo utere nao kuwayeretsa: uwawaze madzi akucotsa zoipa, ndipo apititse lumo pa thupi lao lonse, natsuke zobvala zao, nadziyeretse.

8. Pamenepo atenge ng'ombe yamphongo ndi nsembe yace yaufa, ufa wosanganiza ndi mafuta; utengenso ng'ombe yamphongo yina ikhale nsembe yaucimo.

9. Ndipo ubwere nao Alevi pakhomo pa cihema cokomanako; nuwasonkhanitse khamu lonse la ana a Israyeli;

10. nubwere nao Alevi pamaso pa Yehova; ndi ana a Israyeli aike manja ao pa Alevi;

11. ndi Aroni apereke Alevi ngati nsembe yoweyula pamaso pa Yehova, yocokera kwa ana a Israyeli, kuti akhale akucita nchito ya Yehova,

12. Ndipo Alevi aike manja ao pa mitu ya ng'ombezo; pamenepo ukonze imodzi ikhale nsembe yaucimo, ndi inzace, nsembe yopsereza za Yehova, kucita cotetezera Alevi.

Numeri 8