Numeri 8:3-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Ndipo Aroni anacita cotero; anayatsa nyalizo kuti ziwale pandunji pace pa coikapo nyali, monga Yehova adauza Mose.

4. Ndipo mapangidwe ace a coikapo nyali ndiwo golidi wosula; kuyambira tsinde lace kufikira maluwa ace anacisula; monga mwa maonekedwe ace Yehova anaonetsa Mose, momwemo anacipanga coikapo nyali.

5. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

6. Uwatenge Alevi pakati pa ana a Israyeli, nuwayeretse.

Numeri 8