3. Ndipo Aroni anacita cotero; anayatsa nyalizo kuti ziwale pandunji pace pa coikapo nyali, monga Yehova adauza Mose.
4. Ndipo mapangidwe ace a coikapo nyali ndiwo golidi wosula; kuyambira tsinde lace kufikira maluwa ace anacisula; monga mwa maonekedwe ace Yehova anaonetsa Mose, momwemo anacipanga coikapo nyali.
5. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,
6. Uwatenge Alevi pakati pa ana a Israyeli, nuwayeretse.