Numeri 7:78-81 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

78. Tsiku lakhumi ndi ciwiri kalonga wa ana a Nafitali, ndiye Ahira mwana wa Enani:

79. copereka cace ndico mbizi imodzi yasiliva, kulemera kwace masekeli zana limodzi ndi makumi atatu, mbale yowazira imodzi yasiliva ya masekeli makumi asanu ndi awiri, kuyesa sekeli wa malo opatulika; zonse ziwiri zodzala ndi ufa wosanganiza ndi mafuta, ukhale nsembe yaufa;

80. cipande cimodzi cagolidi ca masekeli khumi, codzala ndi cofukiza;

81. ng'ombe yamphongo imodzi, nkhosa yamphongo imodzi, mwana wa nkhosa mmodzi wa caka cimodzi, zikhale nsembe yopsereza;

Numeri 7