Numeri 7:54-58 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

54. Tsiku lacisanu ndi citatu kalonga wa ana a Manase ndiye Gamaliyeli mwana wa Pedazuri:

55. copereka cace ndico mbizi imodzi yasiliva, kulemera kwace masekeli zana limodzi ndi makumi atatu, mbale yowazira imodzi yasiliva ya masekeli makumi asanu ndi awiri, kuyesa sekeli wa malo opatulika; zonse ziwiri zodzala ndi ufa wosanganiza ndi mafuta, ukhale nsembe yaufa;

56. cipande cimodzi cagolidi ca masekeli khumi, codzala ndi cofukiza;

57. ng'ombe yamphongo imodzi, nkhosa yamphongo imodzi, mwana wa nkhosa mmodzi wa caka cimodzi, zikhale nsembe yopsereza;

58. tonde mmodzi akhale nsembe yaucimo;

Numeri 7