Numeri 6:21-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Ici ndi cilamulo ca Mnaziri wakuwinda, ndi ca copereka cace ca Yehova cifukwa ca kusala kwace, pamodzi naco cimene dzanja lace likacipeza; azicita monga mwa cowinda cace anaciwinda, mwa cilamulo ca kusala.

22. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,

23. Nena ndi Aroni ndi ana ace, ndi kuti, Uzidalitsa ana a Israyeli motero; uziti nao,

24. Yehova akudalitse iwe, nakusunge;

25. Yehova awalitse nkhope yace pa iwe, nakucitire cisomo;

26. Yehova akweze nkhope yace pa iwe, nakupatse mtendere.

27. Potero aike dzina langa pa ana a Israyeli; ndipo ndidzawadalitsa.

Numeri 6