6. Ndipo midziyo muipereke kwa Alevi ndiyd midzi ija isanu ndi umodzi yopulumukirako; imene muipereke kuti wakupha mnzace athawireko; ndipo pamodzi ndi iyi muperekenso midzi makumi anai ndi iwiri.
7. Midzi yonse muipereke kwa Alevi ndiyo midzi makumi anai ndi isanu ndi itatu, iyo pamodzi ndi mabusa ao.
8. Ndipo kunena za midziyo muiperekeyo yao yao ya ana a Israyeli, okhala nayo yambiri mutengeko yambiri; okhala nayo pang'ono mutengeko pang'ono; onse operekako midzi yao kwa Alevi monga mwa colowa cao adacilandira.