Numeri 35:20-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Ndipo akampyoza momkwiyira, kapena kumponyera kanthu momlalira, kuti wafa;

21. kapena kumpanda ndi dzanja lace momuda, kuti wafa, womkanthayo nayenso amuphe ndithu; ndiye wakupha munthu; wolipsa mwazi aphe wakupha munthuyo pomkumika.

22. Koma akampyoza modzidzimuka, osamuda, kapena kumponyera kanthu osamialira,

23. kapena kumponyera mwala wakufetsa munthu, osamuona, namgwetsera uwu, kuti wafa, koma sindiye mdani wace, kapena womfunira coipa;

Numeri 35