17. Kapena akamkantha m'dzanja muli mwala, wakufetsa munthu, ndipo wafa, ndiye wakupha munthu; wakupha munthu nayenso amuphe ndithu.
18. Kapena akamkantha m'dzanja muli cipangizo camtengo, cakufetsa munthu, ndipo wafa, ndiye wakupha munthu; wakupha munthu nayenso amuphe ndithu.
19. Wolipsa mwazi mwini wace aphe wakupha munthuyo; pakumkumika amuphe,
20. Ndipo akampyoza momkwiyira, kapena kumponyera kanthu momlalira, kuti wafa;