Numeri 35:17-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Kapena akamkantha m'dzanja muli mwala, wakufetsa munthu, ndipo wafa, ndiye wakupha munthu; wakupha munthu nayenso amuphe ndithu.

18. Kapena akamkantha m'dzanja muli cipangizo camtengo, cakufetsa munthu, ndipo wafa, ndiye wakupha munthu; wakupha munthu nayenso amuphe ndithu.

19. Wolipsa mwazi mwini wace aphe wakupha munthuyo; pakumkumika amuphe,

20. Ndipo akampyoza momkwiyira, kapena kumponyera kanthu momlalira, kuti wafa;

Numeri 35