Numeri 33:3-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Ndipo anacokera ku Ramese mwezi woyamba, tsiku lakhumi ndi cisanu la mwezi woyamba; atacita Paskha m'mawa mwace ana a Israyeli, anaturuka ndi dzanja lokwezeka pamaso pa Aaigupto onse,

4. pamene Aaigupto ailalikuika oyamba kubadwa ao onse, amene Yehova adawakantha; Yehova adaweruzanso milungu yao.

5. Ndipo ana a Israyeli macokera ku Ramese, nayenda namanga ku Sukoti.

Numeri 33