34. Ndipo ana a Gadi anamanga Diboni, ndi Ataroti, ndi Aroeri;
35. Ataroti Sofani, Yazeri, ndi Yogebeha;
36. ndi Beti Nimira, ndi Beti Harani: midzi ya m'malinga, ndi makola a zoweta.
37. Ndipo ana a Rubeni anamanga Hesiboni, ndi Eleyali, ndi Kiriyataimu;
38. ndi Nebo, ndi Baala Meoni (nasintha maina ao), ndi Sibima; ndipo anaicha midzi adaimanga ndi maina ena.