21. ndi kuoloka Yordano pamaso pa Yehova okonzeka onse mwa inu, kufikira atapitikitsa adani ace pamaso pace,
22. ndi dziko lagonjera Yehova; mutatero mudzabwerere, ndi kukhala osacimwira Yehova ndi Israyeli; ndipo dziko ili lidzakhala lanu lanu pamaso pa Yehova.
23. Koma mukapanda kutero, taonani, mwacimwira Yehova; ndipo zindikirani kuti cimo lanu lidzakupezani.
24. Dzimangireni midzi ya ana anu, ndi makola a zoweta zanu; ndipo muzicite zoturuka m'kamwa mwanu.
25. Ndipo ana a Gadi ndi ana a Rubeni ananena ndi Mose, nati, Anyamata anu adzacita monga mbuyanga alamulira.
26. Ana athu, akazi athu, zoweta zathu, ndi ng'ombe zathu zonse, zidzakhala komweko m'midzi ya ku Gileadi;
27. koma anyamata anu adzaoloka, yense wokonzekera ndi zankhondo pamaso pa Yehova kunkhondo, monga wanena mbuyanga.
28. Pamenepo Mose anamuuza Eleazara wansembe, ndi Yoswa mwana wa Nuni, ndi akuru a makolo a mapfuko a ana a Israyeli za iwo.
29. Ndipo Mose anati kwa iwo, Ngati ana a Gadi ndi ana a Rubeni aoloka nanu Yordano, yense wokonzekera ndi zankhondo pamaso pa Yehova, ndi dziko lagonjera inu; pamenepo muwapatse dziko la Gileadi likhale lao lao;