15. Pakuti mukabwerera m'mbuyo kusamtsata iye, adzawasiyanso m'cipululu, ndipo mudzaononga anthu awa onse.
16. Ndipo anayandikiza, nati, Tidzamangira zoweta zathu makola kuno, ndi ana athu midzi; koma ife tidzakhala okonzeka ndi kufulumira pamaso pa ana a Israyeli, kufikira tidawafikitsa kumalo kwao;
17. ndi ang'ono athu adzakhala m'midzi ya malinga cifukwa ca okhala m'dzikomo.
18. Sitidzabwerera kwathu, kufikira ana a Israyeli atalandira yense colowa cace.