Numeri 30:14-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Koma mwamuna wace akakhala naye cete tsiku ndi tsiku; pamenepo akhazikira zowinda zace zonse, kapena zodziletsa zace zonse, ziri pa iye; wazikhazikitsa, popeza anakhala naye cete tsikuli anazimva iye.

15. Koma akazifafaniza atatha kuzimva; pamenepo adzasenza mphulupulu yace.

16. Awa ndi malemba amene Yehova analamulira Mose, a pakati pa mwamuna ndi mkazi wace, pakati pa atate ndi mwana wace wamkazi, akali namwali, m'nyumba ya atate wace.

Numeri 30