Numeri 29:17-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Ndipo tsiku laciwiri muzibwera nazo ng'ombe zamphongo khumi ndi ziwiri, nkhosa zamphongo ziwiri, ana a nkhosa khumi ndi anai a caka cimodzi, opanda cirema;

18. ndi nsembe yace yaufa, ndi nsembe zace zothira, za ng'ombe, za nkhosa zamphongo, ndi za ana a nkhosa, monga mwa kuwerenga kwace, ndi kutsata lemba lace;

19. ndi tonde mmodzi akhale nsembe yaucimo; pamodzi ndi nsembe yopsereza yosalekeza, ndi nsembe yace yaufa, ndi nsembe zace zothira.

20. Ndi tsiku lacitatu ng'ombe khumi ndi imodzi, nkhosa zamphongo ziwiri, ana a nkhosa khumi ndi anai a caka cimodzi opanda cirema;

Numeri 29