6. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,
7. Ana akazi a Tselofekadi anena zaona; uwapatse ndithu colowa cikhale cao cao pakati pa abale a atate wao; nuwalandiritse colowa ca atate wao.
8. Ndipo unene ndi ana a Israyeli, ndi kuti, Akafa munthu wamwamuna wopanda mwana wamwamuna, colowa cace acilandire mwana wace wamkazi.
9. Ndipo akapanda kukhala naye mwana wamkazi, mupatse abale ace colowa cace.