Numeri 27:6-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

7. Ana akazi a Tselofekadi anena zaona; uwapatse ndithu colowa cikhale cao cao pakati pa abale a atate wao; nuwalandiritse colowa ca atate wao.

8. Ndipo unene ndi ana a Israyeli, ndi kuti, Akafa munthu wamwamuna wopanda mwana wamwamuna, colowa cace acilandire mwana wace wamkazi.

9. Ndipo akapanda kukhala naye mwana wamkazi, mupatse abale ace colowa cace.

Numeri 27