Numeri 27:14-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. popeza munapikisana nao mau anga m'cipululu ca Zini, potsutsana nane khamulo, osandipatula Ine pa madziwo pamaso pao. Ndiwo madzi a Meriba m'Kadesi, m'cipululu ca Zini.

15. Ndipo Mose ananena ndi Yehova, nati,

16. Yehova, Mulungu wa mizimu ya anthu onse, aike munthu pa khamulo,

17. wakuturuka pamaso pao, ndi kulowa pamaso pao, wakuwaturutsa ndi kuwalowetsa; kuti khamu la Ambuye lisakhale ngati nkhosa zopanda mbusa.

Numeri 27