16. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,
17. Sautsa Amidyani ndi kuwakantha;
18. popeza akusautsani ndi manyengo ao amene anakunyengani nao; m'cija ca Peori, ndi ca Kozibi, mwana wamkazi wa kalonga wa ku Midyani, mlongo wao, amene adamupha tsiku la mliri, m'cija ca Peori.