Numeri 21:14-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Cifukwa cace, ananena m'buku la Nkhondo za Yehova,Vahebi m'Sufa,Ndi miyendo ya Arinoni;

15. Ndi zigwa za miyendoyoZakutsikira kwao kwa Ari,Ndi kuyandikizana ndi malire a Moabu.

16. Ndipo atacokapo anamuka ku Been, ndico citsime cimene Yehova anacinena kwa Mose, Sonkhanitsa anthu, ndipo ndidzawapatsa madzi.

17. Pamenepo Israyeli anayimba nyimbo iyi:Tumphuka citsime iwe; mucithirire mang'ombe;

18. Citsime adakumba mafumu,Adacikonza omveka a anthu;Atanena mlamuli, ndi ndodo zao.Ndipo atacoka kucipululu anamuka ku Matana;

Numeri 21