5. Ndipo iwo akumanga mahema ao poyandikizana naye ndiwo a pfuko la Isakara; ndipo kalonga wa ana a Isakara ndiye Netandi mwana wa Zuwara.
6. Ndipo khamu lace, ndi owerengedwa ace, ndiwo zikwi makumi asanu mphambu zinai kudza mazana anai.
7. Ndi pfuko la Zebuloni: kalonga wa ana a Zebuloni ndiye Eliyabu mwana wa Heloni.
8. Ndi khamu lace, ndi owerengedwa ace, ndiwo zikwi makumi asanu mphambu zisanu ndi ziwiri kudza mazana anai.