Numeri 14:41-45 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

41. Ndipo Mose anati, Mutero cifukwa ninji kulakwira mau a Yehova, popeza simudzapindula nako?

42. Musakwereko, pakuti Yehova sali pakati pa inu; kuti angakukantheni adani anu.

43. Pakuti Aamaleki ndi Akanani ali komweko patsogolo panu, ndipo mudzagwa ndi lupanga; popeza mwabwerera m'mbuyo osatsata Yehova, cifukwa cace Yehova sadzakhala nanu.

44. Koma anakwera pamwamba pa phiri modzikuza; koma likasa la cipangano la Yehova, ndi Mose, sanacoka kucigono.

45. Pamenepo anatsika Aamaleki, ndi Akanani, akukhala m'phirimo nawakantha, nawapha kufikira ku Horima.

Numeri 14