13. Ndidzaiona kuti nyama yakuwapatsa anthu awa onse? pakuti amalirira ine, ndi kuti, Tipatseni nyama, tidye.
14. Sinditha kuwasenza anthu awa onse ndekha, pakuti andilemera ine.
15. Ndipo ngati mundicitira cotero, mundiphetu tsopano apa, ngati ndapeza ufulu pamaso panu, ndisayang'ane tsoka langa.
16. Ndipo Yehova anati kwa Mose, Undisonkhanitsire amuna makumi asanu ndi awiri mwa akuru a Israyeli, amene uwadziwa kuti ndiwo akuru a anthu, ndi akapitao ao; nubwere nao ku cihema cokomanako, kuti aimeko pamodzi ndi iwe.