34. Ndipo mtambo wa Yehova unali pamwamba pao msana, pakuyenda iwo kucokera kucigono.
35. Ndipo kunali pakucoka kumka nalo likasa, Mose anati, Ukani Yehova, abalalike adani anu; akuda Inu athawe pamaso panu.
36. Ndi pakupumula ili anati, Bwerani Yehova kwa zikwi zikwi za Israyeli.