Numeri 10:16-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Ndi pa gulu la pfuko la ana a Zebuloni panali Eliyabu mwana wa Heloni.

17. Ndipo anagwetsa kacisi; ndi ana a Gerisoni, ndi ana a Merari, akunyamula kacisi, anamuka naye.

18. Ndi a mbendera ya cigono ca Rubeni, anayenda monga mwa magulu ao; ndipo pa gulu lace anayang'anira Elizuri mwana wa Sedeuri.

Numeri 10