Numeri 1:49-52 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

49. Pfuko la Levi lokha usaliwerenge, kapena kuona kufikira kwao mwa ana a Israyeli;

50. koma iwe, uike Alevi asunge kacisi wa mboni, ndi zipangizo zace zonse, ndi zonse ali nazo; azinyamula kacisi, ndi zipangizo zace zonse; namtumikire, namange mahema ao pozungulira pa kacisi.

51. Ndipo akati amuke naye kacisiyo, Aleviamgwetse, ndipo akati ammange, Alevi amuimike; ndipo mlendo akayandikizako amuphe,

52. Ndipo ana a Israyeli amange mahema ao, yense ku cigono cace, ndi yense ku mbendera yace, monga mwa makamu ao.

Numeri 1