Numeri 1:3-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Iwe ndi Aroni muwawerenge monga mwa magulu ao, onse m'Israyeli akuturuka kunkhondo, kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu,

4. Ndipo pamodzi ndi inu pakhale munthu mmodzi wa mapfuko onse; yense mkuru wa nyumba ya kholo lace.

5. Ndipo maina a amuna amene aime nanu ndi awa: wa Rubeni, Elizuri mwana wa Sedeuri.

6. Wa Simeoni, Selumiyeli mwana wa Zurisadai.

7. Wa Yuda, Nahesoni mwana wa Aminadabu.

Numeri 1