29. Muwakumbukile Mulungu wanga, popeza anadetsa unsembe, ndi pangano la unsembe, ndi la Alevi.
30. Momwemo ndinawayeretsa kuwacotsera acilendo onse, ndi kuikira udikiro ansembe ndi Alevi, yense ku nchito yace;
31. ndi copereka ca nkhuni pa nthawi zoikika, ndi wa zipatso zoyamba. Mundikumbukile, Mulungu wanga, cindikomere.