Nahumu 3:13-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Taona, anthuako m'kati mwako akunga akazi; zipata za dziko lako zatsegulidwira adani ako papakuru; moto watha mipingiridzo yako.

14. Udzitungiretu madzi a nthawi yokumangira misasa, limbikitsa malinga ako, lowa kuthope, ponda dothi, limbitsa ng'anjo yanjerwa.

15. Pomwepo moto udzatha iwe; lupanga lidzakuononga; lidzatha iwe ngati cirimamine; udzicurukitse ngati cirimamine, udzicurukitse ngati dzombe.

16. Wacurukitsa amalonda ako koposa nyenyezi za kuthambo; cirimamine anyambita, nauluka, nathawa.

Nahumu 3