5. Akumbukila omveka ace; akhumudwa m'kupita kwao, afulumira ku linga lace, ndi cocinjiriza cakonzeka.
6. Pa zipata za mitsinje patseguka, ndi cinyumba casungunuka.
7. Catsimikizika, abvulidwa, atengedwa, adzakazi ace alira ngati mau a nkhunda, nadziguguda pacifuwa pao.
8. Koma Nineve wakhala ciyambire cace ngati thamanda lamadzi; koma athawa. Imani, Imani! ati, koma palibe woceuka.
9. Funkhani siliva, funkhani golidi; pakuti palibe kutha kwace kwa zosungikazo, kwa cuma ca zipangizo zofunika ziri zonse.
10. Ndiye mopanda kanthu mwacemo ndi mwacabe, ndi wopasuka; ndi mtima usungunuka, ndi maondo aombana, ndi m'zuuno zonse muwawa, ndi nkhope zao zatumbuluka.