Mlaliki 8:4-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Pakuti mau a mfumu ali ndi mphamvu; ndipo ndani anganene kwa iye, Kodi ucita ciani?

5. Wosunga cilamulo sadzadziwa kanthu koipa; ndipo mtima wa munthu wanzeru udziwa nyengo ndi maweruzo;

6. pakuti kanthu kali konse kali ndi nthawi yace ndi ciweruzo cace; popeza zoipa za munthu zimcurukira;

7. pakuti sadziwa cimene cidzakhala; pakuti ndani angamuuze nthawi yakuti cidzacitidwa?

Mlaliki 8