Mlaliki 7:7-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Indetu nsautso iyarutsa wanzeru; ndi mtulo uipitsa mtima.

8. Citsiriziro ca kanthu ciposa ciyambi cace; wofatsa mtima apambana wodzikuza mtima.

9. Usakangaze mumtima mwako kukwiya; pakuti mkwiyo ugona m'cifuwa ca zitsiru.

10. Usanene, Kodi bwanji masiku akale anapambana ano? Pakuti sulikufunsa mwanzeru pamenepo.

11. Nzeru iri yabwino pamodzi ndi colowa; akuona dzuwa apindula nayo.

12. Pakuti nzeru icinjiriza monga ndalama zicinjiriza; koma kudziwa kupambana, cifukwa nzeru isunga moyo wa eni ace.

13. Tapenya nchito ya Mulungu; pakuti ndani akhoza kulungamitsa comwe iye anacikhotetsa?

Mlaliki 7