15. Ndaona zonsezi masiku anga acabe; pali wolungama angofa m'cilungamo cace, ndipo pali woipa angokhalabe ndi moyo m'kuipa kwace.
16. Usapambanitse kukhala wolungama; usakhale wanzeru koposa; bwanji ufuna kudziononga wekha?
17. Usapambanitse kuipa, ngakhale kupusa, uferenji nthawi yako isanafike?
18. Kuli kwabwino kugwira ici; indetu, usacotsepo dzanja lako pakuti yemwe aopa Mulungu adzaturuka monsemo.
19. Nzeru ilimbitsa wanzeru koposa akuru khumi akulamulira m'mudzi.