Mlaliki 7:15-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Ndaona zonsezi masiku anga acabe; pali wolungama angofa m'cilungamo cace, ndipo pali woipa angokhalabe ndi moyo m'kuipa kwace.

16. Usapambanitse kukhala wolungama; usakhale wanzeru koposa; bwanji ufuna kudziononga wekha?

17. Usapambanitse kuipa, ngakhale kupusa, uferenji nthawi yako isanafike?

18. Kuli kwabwino kugwira ici; indetu, usacotsepo dzanja lako pakuti yemwe aopa Mulungu adzaturuka monsemo.

19. Nzeru ilimbitsa wanzeru koposa akuru khumi akulamulira m'mudzi.

Mlaliki 7