Mlaliki 6:10-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Comwe cinalipo cachedwa dzina lace kale, cidziwika kuti ndiye munthu; sakhoza kulimbana ndi womposa mphamvu.

11. Pokhala zinthu zambiri zingocurukitsa zacabe, kodi anthu aona phindu lanji?

12. Pakuti ndani adziwa comwe ciri cabwino kwa munthu ali ndi moyo masiku onse a moyo wace wacabe umene autsiriza ngati mthunzi? pakuti ndani adzauza munthu cimene cidzaoneka m'tsogolo mwace kunja kuno?

Mlaliki 6