Mlaliki 3:7-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. mphindi yakung'amba ndi mphindi yakusoka; mphindi yakutonthola ndi mphindi yakulankhula;

8. mphindi yakukonda ndi mphindi yakudana; mphindi ya nkhondo ndi mphindi ya mtendere.

9. Wogwira nchito aona phindu lanji m'comsautsaco?

10. Ndaona bvuto limene Mulungu wapatsa ana a anthu kuti abvutidwe nalo.

11. Cinthu ciri conse anacikongoletsa pa mphindi yace; ndipo waika zamuyaya m'mitima yao ndipo palibe munthu angalondetse nchito Mulungu wazipanga ciyambire mpaka citsiriziro.

12. Ndidziwa kuti iwo alibe ubwino, koma kukondwa ndi kucita zabwino pokhala ndi moyo.

Mlaliki 3