Mlaliki 3:6-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. mphindi yakufunafuna ndi mphindi yakumwazika; mphindi yakusunga ndi mphindi yakutaya;

7. mphindi yakung'amba ndi mphindi yakusoka; mphindi yakutonthola ndi mphindi yakulankhula;

8. mphindi yakukonda ndi mphindi yakudana; mphindi ya nkhondo ndi mphindi ya mtendere.

9. Wogwira nchito aona phindu lanji m'comsautsaco?

10. Ndaona bvuto limene Mulungu wapatsa ana a anthu kuti abvutidwe nalo.

Mlaliki 3