Mlaliki 3:15-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Cocomwe cinaoneka, cirikuonekabe; ndi comwe cidzaoneka cinacitidwa kale; Mulungu anasanthula zocitidwa kale.

16. Ndiponso ndinaona kunja kuno malo akuweruza, komweko kuli zaipa; ndi malo a cilungamo, komweko kuli zoipa.

17. Ndinati mumtima wanga, Mulungu adzaweruza wolungama ndi woipa; pakuti pamenepo pali mphindi ya zofuna zonse ndi nchito zonse.

18. Ndinati mumtima mwanga, kuti izi zicitika ndi ana a anthu, kuti Mulungu awayese ndi kuti akazindikire eni ace kuti ndiwo nyama za kuthengo.

Mlaliki 3